Nthawi Lyrics
- Genre:World Music/Folklore
- Year of Release:2022
Lyrics
Nthawi - Lulu & Mathumela Band
...
Nthawi yatha tiyendereni
chikondi Chatha tithandizeni
mukatiyendera zinthu zimayenda
maumboni tili nawo angapo
ndachepa ine,inuyo mukuleeee
mwandilimbisa monga njanji
kusenza zitonzo zochuluka
pa ntchito yomwe inu mudandipasa
ndilinazo ine zitsanzo zambiri
ambiri mudawadusisa
ambiri atchukanso ndi zoipa
zoipa n'kumatandidwa nazo
tilimbiseni ife kukhala m'chiyero
poti n'chifanizo chanufe
Nthawi yatha tiyendereni
chikondi chatha tithandizeni
nkhondo zakuthupi tinayesa
Zina kuwina koma kubwera oguja mano
mbuye wathu tithandizeni
ubale wathu watha tilumikizeni mbuye
madalitso anu abwere ndi mtendere
abale asamapemphe kugwa kwanga
anzanga kumafuna nditagonja
kodi nyumba yawo ya mtundu chani
afuna atagwesa Kaye yanga
mulipo ambuye mulipo
suyu ndili moyo
komabe aphunzitseni azidikira pa inu
Nthawi yatha tiyendereni
chikondi chatha tithandizeni
(nkhondoyi ndi yanu)
nkhondo zakuthupi tinayesa
Zina kuwina koma kubwera oguja mano
mbuye wathu tithandizeni
Asiye machitidwe oti akomere inu Tate
afuna kukomesa za m'dziko owooooh
koma n'kayang'ana nthawi
n'kasanthula malemba
ndi zizindikiro za kumapeto owoowu woh
Nthawi yatha tiyendereni
chikondi chatha tithandizeni
nkhondo zakuthupi tinayesa
zina kuwina koma kubwera oguja mano
mbuye wathu tithandizeni (x3)
Easy and understandable lyric
song sing by Malawian legend(Lulu, Mathumela Band)
Lyric conceded by Chikondi R J Million (From Mj in Malawi)