Lie Lie Lie Lyrics
- Genre:Hip Hop & Rap
- Year of Release:2022
Lyrics
Rebel lions warfare
It's on here
Stand under the music to understand the music
Si ine kazimvelele ongokamba za m`maluwa
Anamva anthuwa
Pa chiyambi panali mawu
Anamveka pa chimkweza mawu
Mwayi wakusintha zinthu nawu
Mphuno salota anawombela mfiti m`manja
Nde ndi ndani andigwile dzanja
Poti zatsimikizika
Zochita za anthu sizisiyanisika
Atupa mimba bwa? atadya zositika
Inu mboba
Boys out here vala zigoba
Anthu oyipa amauvala unjonda
Akaona tsogolo lako lozola komba
Pa maso akonda mu mtima azonda
Amangonama
Tigwetsa mana
Koma zochitika zimasemphana
Kwela pa nsanja zikundu nkumasekana
Dzulo kulonjeza lero kukana
Amangonama
Tigwetsa mana
Koma zochitika zimasemphana
Kwela pa nsanja zikundu nkumasekana
Dzulo kulonjeza lero kukana
Mayi koto m`baleyu si njokaluzi
Pali moto nkulinga utawona utsi
Ali pompo until atapeza nsuzi
Kunyika nsima itamangidwa mu luzi
Nde ndikufunsa
Ena akunena ndikutsutsa
Odya ndiwo ndi ena ife kwathu nkususa
Pali kwina kufasa pali kwina kupusa
Munamupha Mufasa nkani Simba kulusa
Timangomva zama audit zama report
Milandu ingofumbwa kuma court
Ndinamukhulupilira Majoti
Kutaya nkhwali kamba ka manga aka nsoti
Amangonama
Tigwetsa mana
Koma zochitika zimasemphana
Kwela pa nsanja zikundu nkumasekana
Dzulo kulonjeza lero kukana
Amangonama
Tigwetsa mana
Koma zochitika zimasemphana
Kwela pa nsanja zikundu nkumasekana
Dzulo kulonjeza lero kukana
Kutipaka nsuzi nkutijambula odya ena
Ndithudi muzakumana nayo gahena
Ankabwela pano tikawaona mpakanema
Mbiri ndiya khoswe kadya nkena
Tinamva manifesto
Kalata ya Paulo yolembela Aefeso
Tonse kukhala mtundu koma munthu ndi chileso
M`mutu modzadza mfundu ati vuto ndi chipeso
Yesa ulonjezenso
Ndi mabodza omveka bwino tatengeka
Chilungamo chenicheni tanyengeka
Ochepa za wayendela ambiri tapweteka
Amphawi taoneleledwa tapezeka
Amangonama
Tigwetsa mana
Koma zochitika zimasemphana
Kwela pa nsanja zikundu nkumasekana
Dzulo kulonjeza lero kukana
Amangonama
Tigwetsa mana
Koma zochitika zimasemphana
Kwela pa nsanja zikundu nkumasekana
Dzulo kulonjeza lero kukana